< Lucas 12 >

1 Y sasta se terelasen catanado al crugos de Jesus baribustri sueti, de modo que yeques á averes bucharelaban ostely, se chitó á penar á desqueres discipules: Garabelaos de la levadura es Phariseyes, que sinela jujana.
Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.
2 Na sinela buchi ucharada, sos na se haya de dicar: ni buchi escondida, sos na se haya de chanelar.
Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
3 Presas as buchias, que penasteis andré a rachi, á la dut sinarán chamuliadas: y ma chamulasteis á la cani andré os queres, sinará pucanado opré os tejados.
Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
4 A sangue pues plalores de mangue os penelo: Que na tereleis dal de ocolas, sos marelan o trupos, y despues de ocono, na terelan butér que querelar.
“Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu.
5 Tami menda penaré sangue á coin jomte terelar dal: Terelad dal á ocola, sos despues de nicobar a chipen, terela ezor de bucharar al butron: andiar sangue penelo, a ocona terelad dal. (Geenna g1067)
Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna g1067)
6 ¿Na se binelan pansch ujarres por dui calés, y yeque de ocolas na sinela olvidado anglal de Debél?
Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu.
7 Y aun as balas de jire jero sarias sinelan jinadas. Pues na darañeleis: presas amolelais baribu butér, que ujarres baribustres.
Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
8 Y tambien sangue penelo, Que o saro manu sos veáre mangue anglal es manuces, o Chaboro e manu lo veará tambien á ó anglal es Manfarieles de Debél.
“Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu.
9 Tami ó sos me negisáre anglal es manuces, negado sinará anglal es Manfarieles de Debél.
Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu.
10 Y o saro manu sos chibare abrí yeque varda contra o Chaboro e manu, ertinado le sinará: Tami á ocola sos penáre zermañas contra o Peniche, na le sinará ertinado, nanai.
Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.
11 Y pur sangue lligueraren á as Synagogas, y á os Chineles, y a os Solares, na piraleis penchabando, sasta, ó qué terelais de rudelar, o penar.
“Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule,
12 Presas o Ducos Majaro sangue penará andré ocola ocana ma sangue jomte penar.
pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”
13 Y yeque de la sueti le penó: Duquendio, pen á minrio plal que partisarele con-a-mangue la jayere.
Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”
14 Tami ó le rudeló: ¿Manu, coin ha childo mangue por Barander o repartidor enré sangue?
Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?”
15 Y les penó: Diquelad, y garabelaos de sari cascañia: presas a chipen de saro yeque no sinela andré la baribustri es buchias sos terela.
Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
16 Y les penó yeque parabola, penando: La pu de yeque manu balbalo habia diñado mibao baribu.
Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri.
17 Y ó penchababa enré sí matejo, y penaba: ¿Qué querelaré, presas na terelo anduque pandisarar minrio mibao?
Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’
18 Y penó: Ocono querelaré: Buchararé abajines minres malabayes, y os querelaré mas bares: y oté chibaré saro minrio mibao, y minres balbalipenes.
“Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu.
19 Y penaré á minri ochi: Ochi, baribustres balbalipenes terelas chités para baribustres berjis: Sobela, jama, piya, din jachipenes.
Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’”
20 Tami Debél le penó: Dinelo, ocona rachi te vuelven á ustilar a ochi, ¿Ma has chitó, para coin sinará?
“Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’
21 Andiar sinela ó sos chitela manchin para sí; y na sinela balbalo andré Debél.
“Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”
22 Y penó á os discipules de ó: Pre ocono sangue penelo: na pireleis solicitos para jiré ochi, ma jamareis, ni para o trupos, que coneles chibareís.
Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
23 Butér sinela a ochi, que o jamar, y o trupos que os coneles.
Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala.
24 Diquelad os cuerves, sos na chinelan, ni terelan dispensa, ni malabai, y Debél os parbarela. ¿Pues quanto butér amolelais sangue que junos?
Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
25 Y coin de sangue, por baribu que lo penchabele, astisarela chibar a sun estatura yeque codo butér?
Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
26 Pues si na astisarelais ma sinela mendesquero: ¿por qué pireleis penchabando por as avérias buchias?
Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?
27 Diquelad os lirios sasta se querelan baro; sos ni randiñelan ni hilan: pues sangue penelo, que ni Salomon andré saro desquero chimusolano, na sinaba tan chitó sasta yeque de oconas.
“Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa.
28 Pues si al cha, sos achibes sinela andré o lugos, y tasata se bucharela andré o sosimbo, Debél vistió andiar lacho; ¿quanto butér á sangue de frima fé?
Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
29 Na pireleis pues penchabando andré ma terelais de jamar, o piyar, y na pireleis ardiñelados.
Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
30 Presas sarias oconas sinelan buchias, en que pirelan penchabando os busnes de la sueti. Y jire Dada chanela, que de oconas terelais necesidad.
Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi.
31 Pre ocono orotelad brotobo o chim de Debél, y su lachoria; y sarias oconas buchias á sangue sinarán jinadas.
Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
32 Na darañeleis, ne-bari plastañi; presas jire Dada ha camelado diñaros o chim.
“Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
33 Binelad ma terelais y diñad limosna. Querelaos quisobes, sos na se chitelan purés, manchin andré o Charos, sos jamas faltisarela: anduque o rande na bigorela, y na jamela a polilla.
Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge.
34 Presas duque sinela jire manchin, oté tambien sinará jire carlochin.
Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
35 Terelad ceñidos jires dumes, y mermellines encendidas andré jires bastes.
“Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka,
36 Y sinelad sangue semejantes á os manuces, sos ujarelan á o Erañó de junos, pur limbidiela de las romandiñipenes: somia que pur abilláre, y araqueráre á la bundal, yescotria le pindrabelen.
ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko.
37 Majarés ocolas lacrés, sos alacháre velando o Erañó pur abilláre: Aromali sangue penelo, que se chibará la sustigui; y os querelará bestelar á la mensalle, y nacando os servirá.
Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira.
38 Y si abilláre andré la duisquera vela, y si abilláre andré la trinchera vela, y andiar alacháre á junos, majarés sinelan oconas lacrés.
Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku.
39 Tami chanelad ocono, que si o julai e quer chanelase a ocana en que abillaria o randé, na querelaria o sobindoi, y na mequelaria enquerar su quer.
Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
40 Sangue pues sinelad emposunés: presas á la ocana, que na penchabelais, abillará o Chaboro e manu.
Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
41 Y Pedro le penó: Erañó, penelas ocona parabola á amangue, ó tambien á os sares.
Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
42 Y penó o Erañó, ¿Coin, penchabelais que sinela o baro-lacró lacho y cabalico, sos chitó o Erañó opré su sueti, somia que les díñele o melalo de gi andré chiros?
Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera?
43 Majaro ocola lacró, sos pur abilláre o Erañó, le alacháre andiar querelando.
Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.
44 Aromali sangue penelo, que lo chitará opré saro que terela.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
45 Tami si penáre ocola lacro andré su carló: Se tasalela minrio Erañó de abillar, y se chibáre á querelar choro á os lacrés, y á as lacrias, y á jamar, y á pijar, y diñarse á curdá:
Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera.
46 Abillará o Erañó de ocola lacró o chibes, que na penchabela, y á la ocana que na chanela, y le chibará abrí, y chitará su aricata sat junos de dabrocos.
Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
47 Presas ocola lacró sos chanó ma camelaba desquero Erañó, y na queró bajin, y na queró ma camelaba, sinará muy mistos curado.
“Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri.
48 Tami ó sos na chanó, y queró buchias dignas e saniséo, frima sinará curado: presas á saro manu, á coin baribu sinaba diñado; baribu le sinará manguelado: y al que baribu encomendáron, butér le ustilarán.
Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
49 Yaque he abillado á chitar andré la pu: ¿y que camelo, sino que jacharele?
“Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale.
50 Me jomte sinelar chobelado sat bautismo: ¿y cómo me trajatelo, disde que se lo querele?
Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika!
51 ¿Penchabelais, que sinelo abillado á chitar paz andré la pu? Sangue penelo que nanai, sino chingaripen.
Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana.
52 Presas de acoi anglal sinarán pansch andré yeque quer en chingaripen, os trin sinarán contra os dui, y os dui contra os trin.
Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu.
53 Sinarán en chingaripen o batu sat o chaboro; la dai sa’ la chabori, y la chabori sa’ la dai, la dai e rom sa’ la romi, y la romi sa’ la dai e rom.
Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”
54 Y penaba tambien á la sueti: pur diquelais ardiñelar o paros del aracata e poniente, yescotria penelais: Buros abillela: y andiar anaquela.
Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi.
55 Y pur chumasquerela o Austro, penelais: jar querelará: y chachipen sinela.
Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi.
56 Sungalés, chanelais distinguir as chichias e charos y de la pu: ¿pues como na chanelais pincherar o chiros presente?
Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?
57 ¿Y por qué na pincherelais por sangue matejos: ma sinela lacho?
“Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita?
58 Pur chalas sa’ tun daschmanu al Manclay, querela ma astis somia listrabarte de ó andré o drun, somia que na te lliguerele al Barander, y o Barander te díñele al chinel, y o chinel te chitele andré l’estaripel.
Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende.
59 Te penelo, que na chalarás abrí de acoi, disde que poquineles o segriton cale.
Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”

< Lucas 12 >