< 3 Царе 21 >

1 След тия събития, понеже езраелецът Навутей имаше лозе в Езраил, близо до палата на самарийския цар Ахаава,
Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
2 Ахаав говори на Навутея казвайки: Дай ми лозето си да го имам за бостан, понеже е близо до къщата ми; и вместо него ще ти дам лозе по-добро от него, или, ако ти се види добре, ще ти дам стойността му в пари.
Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
3 А Навутей рече на Ахаава: Да ми не даде Господ да ти дам бащиното си наследство.
Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
4 И Ахаав дойде у дома си тъжен и огорчен поради думата, която езраелецът Навутей му каза, като рече: Не ща да ти дам бащиното си наследство. И като легна на леглото си, отвърна лицето си и не яде хляб.
Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
5 Тогава жена му Езавел дойде при него та му рече: Защо е духът ти тъжен, та не ядеш хляб?
Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
6 А той каза: Понеже говорейки на езраелеца Навутей рекох му: Дай ми лозето си с пари, или, ако обичаш, ще ти дам друго лозе вместо него; а той отговори: Не ща да ти дам лозето си.
Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
7 А жена му Езавел му рече: Царуваш ли ти наистина над Израиля? Стани, яж хляб, и нека е весело на сърцето ти; аз ще ти дам лозето на езраелеца Навутей.
Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
8 И така, тя писа писма от Ахаавово име, и като ги запечата с печата му, прати писмата до старейшините и благородните, които бяха в града му, живеещи с Навутея.
Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
9 В писмата писа, казвайки: Прогласете пост, и поставете Навутея на видно място пред людете;
Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
10 и срещу него поставете двама лоши човеци да засвидетелствуват против него казвайки: Ти похули Бога и царя. Тогава го изведете вън и убийте го с камъни, и нека умре.
Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
11 И мъжете от града му, старейшините и благородниците, които живееха в града му, сториха според заповедта, която Езавел им бе пратила, според написаното в писмата, които им бе пратила;
Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
12 прогласиха пост, и поставиха Навутея на видно място пред людете.
Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
13 И двамата лоши човеци влязоха и седнаха пред него; и лошите човеци свидетелствуваха против него, против Навутея, пред людете, казвайки: Навутей похули Бога и царя. Тогава го изведоха вън от града, та го убиха с камъни; и умря.
Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
14 После пратиха да Езавел да кажат: Навутей е убит с камъни и умря.
Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
15 И като чу Езавел, че Навутей бил убит с камъни и умрял, Езавел рече на Ахаава: Стани, присвои си лозето, което езраелецът Навутей отказа да ти даде с пари; защото Навутей не е жив, но е умрял.
Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
16 И като чу Ахаав, че Навутей е умрял, Ахаав стана та слезе в лозето на езраелеца Навутей за да го присвои.
Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
17 Но Господното слово дойде към тесвиеца Илия и рече:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
18 Стани, слез да посрещнеш Израилевия цар Ахаава, който живее в Самария; ето, той е в Навутеевото лозе, гдето слезе да го присвои.
“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
19 И да му говориш казвайки: Така казва Господ: Уби ли ти, а още присвои ли ти? Да му говориш още казвайки: Така казва Господ: На мястото, гдето кучетата лизаха Навутеевата кръв, кучетата ще лижат твоята кръв, да! твоята.
Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
20 А Ахаава каза на Илия: Намери ли ме, враже мой? А той отговори: Намерих те, защото ти си продал себе си да вършиш зло пред Господа.
Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
21 Ето казва Господ: Аз ще докарам зло върху тебе, ще те измета, и ще изтребя от Ахаава всеки от мъжки пол, както малолетния, така и пълнолетния в Израиля;
Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
22 и ще направя дома ти като дома на Еровоама Наватовия син, и като дома на Вааса Ахиевия син, поради раздразнението, с което Ме ти разгневи, като направи Израиля да съгреши.
Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
23 Също и на Езавел говори Господ, казвайки: Кучетата ще изядат Езавел при рова на Езраел.
“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
24 Който от Ахаавовия род умре в града, него кучетата ще изядат; а който умре в полето, него въздушните птици ще изядат.
“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
25 (Никой, наистина, не биде подобен на Ахаава, който продаде себе си да върши зло пред Господа, като го подбуждаше жена му Езавел,
(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
26 и който извърши много мерзости, като следваше идолите, съвсем, както вършеха аморейците, които Господ бе изгонил пред израилтяните).
Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
27 А Ахаав, като чу тия думи, раздра дрехите си, тури вретище на снагата си, пости и лежеше обвит във вретище, и ходеше внимателно.
Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
28 Тогава Господното слово дойде към тесвиеца Илия и рече:
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
29 Видя ли как се смири Ахаав пред Мене? Понеже той се смири пред Мене, няма да докарам злото в неговите дни; в дните на сина му ще докарам злото върху дома му.
“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

< 3 Царе 21 >