< 1 कुरिन्थियों 3 >

1 हे ढ्लाव ते बेइनव, ज़ैखन अवं तुसन कां थियो त तुसन सेइं एन्च़रे सब गल्लां न केरि बटो, ज़ेन्च़रे आत्मिक लोकन सेइं; पन ज़ेन्च़रे तैन सेइं ज़ैना मसीह मां बच्चेन।
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 मीं तुसन परमेशरेरे वचने मरां सिर्फ बुनियादी गल्लां केरि शिक्षा दित्ती ते डुग्घी सच़्च़ाई नईं। किजोकि तैस वक्ते तुस तै शिक्षा हासिल केरनेरे ते समझ़नेरे काबल न थिये, बल्के हेजू भी हासिल केरनेरे काबल नईं।
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 किजोकि हेजू तगर भी गैर विश्वासी केरे ज़ेरे आथ। एल्हेरेलेइ कि ज़ैखन तुसन मां बैर, ते लड़ाइयन, त कुन तुस गैर विश्वासी केरे ज़ेरे न भोए? तुस एरे लोकां केरि ज़ेरि ज़िन्दगी ज़ींने लोरेथ, ज़ैन केरो रिश्तो प्रभु सेइं न भोए।
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 एल्हेरेलेइ अक ज़ोते, “अवं पौलुसेरोईं,” ते होरो ज़ोते, “अवं अपुल्लोसेरो आईं,” त कुन तुस एरे लोकां केरि ज़ेरि ज़िन्दगी ज़ींने बाले न भोए, ज़ैन केरो रिश्तो प्रभु सेइं न भोए!
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 अपुल्लोस कौने? ते पौलुस कौने? सिर्फ सेवक, ज़ैन केरे ज़िरिये तुसेईं प्रभु पुड़ विश्वास कियो, असन मरां हर केन्चे कम कियूं ज़ेन्च़रे परमेशरे केरनेरे लेइ दित्तू।
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 अगर अवं तुश्शी तुलना ऊडारे सेइं केरि त मीं बीज़ बेवं, अपुल्लोसे सग्गू, पन परमेशरे बडावं।
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 एल्हेरेलेइ न त लानेबालो किछे, ते न सग्गने बालो किछे, पन परमेशर ज़ै बडाने बालोए।
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 लानेबालो ते सग्गने बालो दुइये अक्कन; पन हर मैन्हु अपने-अपने मज़दूरारो फल मैलनोए।
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 किजोकि अस परमेशरे सेइं साथी कम केरनेबाले आम, तुस एरे ऊडारां केरे ज़ेरे आथ ज़ैन केरो तलक परमेशरे सेइं आए, ते इसेरे आलाव तुश्शी तुलना एरे घरे सेइं केरताईं ज़ैन परमेशरे बनावरूए।
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 परमेशरे ज़ैन कम मीं केरनेरे लेइ दितोरू थियूं, मीं तैन अक्लमन्दी सेइं कियूं; अवं माहिर मिस्रेरो ज़ेरो आईं, मीं तुश्शे नगरे मां खुशखबरी प्रचार की ते शुरू मां तुसन यीशु पुड़ विश्वास केरनेरे लेइ मद्दत की, तैट्ठां बाद ज़ैस कम्मेरी शुरुआत मीं कियोरी थी, होरे मसीही सेवा केरनेबाले तैस बुनियादी पुड़ लगातार कम केरते राए। पन असन मरां हर एक्की कम केरनेबाले ध्याने सेइं सोचोरू लोड़े, कि असेईं परमेशरेरू कम केन्च़रे लोड़े कियोरू।
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 किजोकि यीशु मसीह सच़्च़ी बुनीयाद आए, ते होरो कोई होरि बुनीयाद न बनेइ सके, तैन इन आए, कोई तुसन मुक्ति हासिल केरनेरे लेइ नव्वीं शिक्षा न शिखैली बटे, मीं तुसन सेइं पेइलू ज़ोवरू कि परमेशर असन यीशु मसीहेरे ज़िरिये मुक्ति देते।
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 ते अगर कोई इस मुनीयादी पुड़ सोन्नू चाँदी या कीमती घोड़ या कैड़ु या घास फूसेरो रद्दो रखते।
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 ज़ैखन मसीह फिरी वापस एज्जेलो, त अग हर एक्केरे कम्मे परखेली, ते अग हर मैनेरे कम्मेरी कीमत हिराली।
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 ज़ेसेरू कम तैस अग्गी सेइं न फुकोलू, तैस मज़दूरी मैलनीए।
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 ते अगर केन्चेरू कम फुकोलू, त तैस नुकसान भोलो; पन तै एप्पू बच़नोए पन फुकोते-फुकोते।
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 कुन तुस न ज़ानथ, कि तुस परमेशरेरू मन्दरथ, ते परमेशरेरो आत्मा तुसन मां रहते?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 अगर कोई तुसन नुकसान पुज़ाए, त परमेशर तैस नाश केरेलो; किजोकि परमेशरेरू मन्दर पवित्रे, ते तैन तुस आथ।
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 कोई अपने आपे धोखो न दे, अगर तुसन मरां कोई इस दुनियारे लोकन मां अपनो आप अक्लमन्द समझ़े, त तैस दुनियारी नज़री मां बेवकूफ बनोरू लोड़े; ताके परमेशरेरे नज़री मां सच़्च़े ज्ञानी बने। (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 किजोकि इस दुनियारी अक्ल परमेशरे कां बेवकूफीए, ज़ेन्च़रे पवित्रशास्त्रे मां लिखोरूए; “परमेशर ज्ञैन्न तैन केरे च़लैकी मां फसाते।”
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 ते फिरी पवित्रशास्त्र इन भी ज़ोते, “प्रभु ज्ञैनी केरे खियालन ज़ानते कि बेफैइदेन।”
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 एल्हेरेलेइ कोई मैनन् पुड़ घमण्ड न केरे, किजोकि किछ परमेशरे तुश्शू भलेरे लेइ दित्तोरूए।
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 तैन इन आए कुन अवं पौलुस, कुन अपुल्लोस, कुन कैफा, कुन दुनिया, कुन ज़ीनू, कुन मरनू, कुन ई वक्त, कुन एजनेबालो वक्त, सब किछ तुश्शूए।
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 ते तुस मसीहेरेथ, ते मसीह परमेशरेरोए।
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 कुरिन्थियों 3 >