< 1 Golidia 3 >

1 Be na fi dunu! Na da dunu ilia Gode Ea A: silibu lai dagoi ilima sia: mu, amo defele na da dilima sia: mu gogolei. Na da osobo bagade dunu, mano dudubusa Gelesu Ea hou lalegagui dunu ilima sia: sa defele dilima sia: i.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 Na da dilima gasa ha: i manu mae iawane, dodo hano fawane iasu. Bai dilia da gasa ha: i manu, manu hamedei. Amola wali, dilia amo manu hamedei.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 Bai dilia da osobo bagade dunu ilia hou defele hamonana. Dilia da mudasu amola sia: ga gegesu hamonanebeba: le, dilia da osobo bagade dunu defele esala amo olelesa.
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 Afadafa da amane sia: sa, “Na da Boloma fa: no bobogesa!” Eno da amane sia: sa, “Na da Abolesema fa: no bobogesa!” Agoane hamobeba: le, dilia da osobo bagade hame lalegagui dunu defele hamosa.
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Abolose da nowala: ? Bolo da nowala: ? Ania da Gode Ea hawa: hamosu dunu fawane. Ania da hawa: hamobeba: le, Gode da dilima dafawaneyale dawa: su hou olelei. Ninia da Hina Gode Ea ilegei hawa: hamosu fawane hamonana.
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 Na da hawa: bugi. Abolose da amoma hano soga: su. Be Gode Hi fawane da amo bugi sono heda: ma: ne hamosu.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 Hawa: bugisu dunu amola hano soga: su dunu da dunu hamedei agoane. Be Gode Hi fawane da bugi heda: ma: ne hamobeba: le, Hi hou da bagadedafa.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 Hawa: bugisu dunu amola hano soga: su dunu da hisu hisu hame. Gode da dunu huluane ilia hawa: hamoi hisu hisu, amo defele ilima bidi imunu.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 Ania da gilisili Gode Ea hawa: hamonana. Dilia da fedege agoane Gode Ea sagai gala. Dilia da Gode Ea diasu.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 Gode da nama dawa: su hou iabeba: le, na da diasu gagusu dunu ida: iwane gala ea hou defele, diasu ifa bugi dagoi. Dunu eno da amo diasu ifa bai da: iya diasu gagusa. Be dunu huluane da dawa: iwane diasu gagumu da defea.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 Gode da diasu gaguma: ne, diasu ifa baidafa afadafa fawane amo Yesu Gelesu, Gode da bugi dagoi. Gode Ea diasu gaguma: ne, diasu ifa bai eno bugimu hame gala, Yesu Gelesu Hi fawane.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Dunu mogili, diasu gaguma: ne, ilia amo diasu bai da: iya gouli, silifa, igi ida: iwane gala amola ouli amo bai da: iya gagusa. Be eno ilia wadela: i ifa, gisi amola me, amoga diasu gagusa.
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 Be Yesu Gelesu Ea bu misunu eso amoga, E da dunu huluane ilia gagusu hou adoba: mu. Bai amo esoga, lalu da dunu huluane ilia hawa: hamoi hou huluane adoba: mu.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 Nowa dunu da diasu bai da: iya diasu gasa bagade gagui ba: sea, gagusu dunu da bidi ida: iwane lamu.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 Be nowa da diasu gasa hame gagui ba: sea, ea diasu da laluga nei dagole, hawa: hamoi fisimu. Be Gode da amo dunu gaga: mu. Be e da fedege agoane, abula nene dagole, da: i nabadowane Gode Ea sogega heda: mu.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Dilia da Gode Ea Debolo Diasu gala, amola Gode Ea A: silibu Hadigidafa Gala da dilia da: i hodo ganodini esala. Amo dilia dawa: bela: ?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 Amaiba: le, nowa da Gode Ea Debolo Diasu wadela: sea, Gode da amo dunu wadela: mu. Gode Ea Debolo Diasu da hadigi gala amola dili da Gode Ea Debolo Diasu.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Dilia hou dilisu mae ogogoma! Nowa dunu da osobo bagade hou dawa: beba: le, hi da na bagade dawa: su hisu da dawa: sea, defea, amo dunu da ea hou fonobone, gagaoui agoane hamomu da defea. Amasea, e da bagade dawa: sudafa bu ba: mu. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 Bai osobo bagade dunu ilia bagade dawa: su ba: su liligi, amo Gode da gagaoui liligi agoane ba: sa. Gode Sia: Dedei defele, “Gode da bagade dawa: su dunu ilia bagade dawa: su hou afadenene bu ilima sani agoane hamosa!”
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 Gode Sia: eno da agoane dedei diala, “Hina Gode da bagade dawa: su dunu ilia asigi dawa: su da hamedei liligi dawa:”
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Amaiba: le, ninia da osobo bagade dunu ilia hawa: hamobeba: le hidale sia: mu da defea hame. Liligi huluane da dilia liligi gala.
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 Bolo, Abolose, Bida, osobo bagade, esalusu, bogosu, wali eso amola fa: no misunu eso, - liligi huluane da dilia liligi.
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 Amola dili da Yesu Gelesu Ea: Amola Yesu Gelesu da Gode Ea:
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Golidia 3 >