< ܥܒܪ̈ܝܐ 12 >

ܡܛܠ ܗܢܐ ܐܦ ܚܢܢ ܕܐܝܬ ܠܢ ܗܠܝܢ ܟܠܗܘܢ ܤܗܕܐ ܕܐܝܟ ܥܢܢܐ ܚܕܝܪܝܢ ܠܢ ܢܫܕܐ ܡܢܢ ܟܠ ܝܘܩܪܝܢ ܐܦ ܚܛܝܬܐ ܕܒܟܠܙܒܢ ܡܛܝܒܐ ܗܝ ܠܢ ܘܒܡܤܝܒܪܢܘܬܐ ܢܪܗܛܝܘܗܝ ܠܐܓܘܢܐ ܗܢܐ ܕܤܝܡ ܠܢ 1
Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.
ܘܢܚܘܪ ܒܝܫܘܥ ܕܗܘ ܗܘܐ ܪܝܫܐ ܘܓܡܘܪܐ ܠܗܝܡܢܘܬܢ ܕܚܠܦ ܚܕܘܬܐ ܕܐܝܬ ܗܘܐ ܠܗ ܤܝܒܪ ܨܠܝܒܐ ܘܥܠ ܒܗܬܬܐ ܐܡܤܪ ܘܥܠ ܝܡܝܢܐ ܕܟܘܪܤܝܗ ܕܐܠܗܐ ܝܬܒ 2
Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu.
ܚܙܘ ܗܟܝܠ ܟܡܐ ܤܝܒܪ ܡܢ ܚܛܝܐ ܗܢܘܢ ܕܗܢܘܢ ܗܘܘ ܤܩܘܒܠܐ ܠܢܦܫܗܘܢ ܕܠܐ ܬܡܐܢ ܠܟܘܢ ܘܠܐ ܬܬܪܦܐ ܢܦܫܟܘܢ 3
Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima.
ܠܐ ܥܕܟܝܠ ܡܛܝܬܘܢ ܥܕܡܐ ܠܕܡܐ ܒܐܓܘܢܐ ܕܠܘܩܒܠ ܚܛܝܬܐ 4
Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.
ܘܛܥܝܬܘܢܝܗܝ ܠܝܘܠܦܢܐ ܐܝܢܐ ܕܐܝܟ ܕܠܒܢܝܐ ܐܡܪ ܠܟܘܢ ܒܪܝ ܠܐ ܬܗܡܐ ܡܢ ܡܪܕܘܬܗ ܕܡܪܝܐ ܘܠܐ ܬܪܦܐ ܢܦܫܟ ܐܡܬܝ ܕܡܢܗ ܡܬܟܘܢ ܐܢܬ 5
Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa: “Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.
ܠܡܢ ܕܪܚܡ ܓܝܪ ܡܪܝܐ ܪܕܐ ܠܗ ܘܡܢܓܕ ܠܒܢܝܐ ܐܝܠܝܢ ܕܗܘ ܨܒܐ ܒܗܘܢ 6
Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”
ܤܝܒܪܘ ܗܟܝܠ ܡܪܕܘܬܐ ܡܛܠ ܕܐܝܟ ܕܠܘܬ ܒܢܝܐ ܤܥܪ ܨܐܕܝܟܘܢ ܐܠܗܐ ܐܝܢܘ ܓܝܪ ܒܪܐ ܕܠܐ ܪܕܐ ܠܗ ܐܒܘܗܝ 7
Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga?
ܘܐܢ ܕܠܐ ܡܪܕܘܬܐ ܐܢܬܘܢ ܗܝ ܕܒܗ ܡܬܪܕܐ ܟܠܢܫ ܗܘܝܬܘܢ ܠܟܘܢ ܢܘܟܪܝܐ ܘܠܐ ܒܢܝܐ 8
Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo.
ܘܐܢ ܐܒܗܝܢ ܕܒܤܪܐ ܪܕܝܢ ܗܘܘ ܠܢ ܘܒܗܬܝܢ ܗܘܝܢ ܡܢܗܘܢ ܟܡܐ ܗܟܝܠ ܚܝܒܝܢܢ ܕܢܫܬܥܒܕ ܠܐܒܘܗܝܢ ܕܪܘܚܬܐ ܘܢܚܐ 9
Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo?
ܗܢܘܢ ܓܝܪ ܠܙܒܢ ܗܘ ܙܥܘܪ ܐܝܟ ܕܨܒܝܢ ܗܘܘ ܪܕܝܢ ܗܘܘ ܠܢ ܐܠܗܐ ܕܝܢ ܠܥܘܕܪܢܢ ܕܢܫܬܘܬܦ ܠܩܕܝܫܘܬܗ 10
Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima.
ܟܠ ܡܪܕܘܬܐ ܕܝܢ ܒܙܒܢܗ ܠܐ ܡܤܬܒܪܐ ܕܕܚܕܘܬܐ ܗܝ ܐܠܐ ܕܟܪܝܘܬܐ ܠܚܪܬܐ ܕܝܢ ܦܐܪܐ ܕܫܠܡܐ ܘܕܙܕܝܩܘܬܐ ܝܗܒܐ ܠܐܝܠܝܢ ܕܒܗ ܐܬܕܪܫܘ 11
Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.
ܡܛܠ ܗܢܐ ܐܝܕܝܟܘܢ ܡܫܪܝܬܐ ܘܒܘܪܟܝܟܘܢ ܪܥܠܬܐ ܫܪܪܘ 12
Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka.
ܘܫܒܝܠܐ ܬܪܝܨܐ ܥܒܕܘ ܠܪܓܠܝܟܘܢ ܕܗܕܡܐ ܕܚܓܝܪ ܠܐ ܢܛܥܫ ܐܠܐ ܢܬܐܤܐ 13
Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.
ܗܪܛܘ ܒܬܪ ܫܠܡܐ ܥܡ ܟܠ ܐܢܫ ܘܒܬܪ ܩܕܝܫܘܬܐ ܕܒܠܥܕܝܗ ܐܢܫ ܠܡܪܢ ܠܐ ܚܙܐ 14
Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye.
ܘܗܘܝܬܘܢ ܙܗܝܪܝܢ ܕܠܡܐ ܐܢܫ ܢܫܬܟܚ ܒܟܘܢ ܕܚܤܝܪ ܡܢ ܛܝܒܘܬܐ ܕܐܠܗܐ ܐܘ ܕܠܡܐ ܥܩܪܐ ܕܡܪܪܐ ܢܦܩ ܥܘܦܝܐ ܘܢܗܪܟܘܢ ܘܒܗ ܤܓܝܐܐ ܢܤܬܝܒܘܢ 15
Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri.
ܐܘ ܠܡܐ ܐܢܫ ܢܫܬܟܚ ܒܟܘܢ ܕܙܢܝ ܘܪܦܐ ܐܝܟ ܥܤܘ ܕܒܚܕܐ ܡܐܟܘܠܬܐ ܙܒܢ ܒܘܟܪܘܬܗ 16
Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake.
ܝܕܥܝܢ ܐܢܬܘܢ ܓܝܪ ܕܐܦ ܡܢ ܒܬܪܟܢ ܨܒܐ ܗܘܐ ܕܢܐܪܬ ܒܘܪܟܬܐ ܘܐܤܬܠܝ ܐܬܪܐ ܓܝܪ ܠܬܝܒܘܬܐ ܠܐ ܐܫܟܚ ܟܕ ܒܕܡܥܐ ܒܥܗ 17
Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.
ܠܐ ܓܝܪ ܐܬܩܪܒܬܘܢ ܠܢܘܪܐ ܕܝܩܕܐ ܘܡܬܓܫܐ ܐܦܠܐ ܠܚܫܘܟܐ ܘܠܥܪܦܠܐ ܘܠܥܪܘܪܐ 18
Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho;
ܘܠܐ ܠܩܠܐ ܕܩܪܢܐ ܘܠܩܠܐ ܕܡܠܐ ܗܘ ܕܗܢܘܢ ܕܫܡܥܘܗܝ ܐܫܬܐܠܘ ܕܠܐ ܢܬܬܘܤܦ ܢܬܡܠܠ ܥܡܗܘܢ 19
limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena.
ܠܐ ܓܝܪ ܡܫܟܚܝܢ ܗܘܘ ܠܡܤܝܒܪܘ ܡܕܡ ܕܐܬܦܩܕܘ ܕܐܦܢ ܚܝܘܬܐ ܬܬܩܪܒ ܠܘܬ ܛܘܪܐ ܬܬܪܓܡ 20
Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.”
ܘܗܟܢܐ ܕܚܝܠ ܗܘܐ ܚܙܘܐ ܕܡܘܫܐ ܐܡܪ ܕܕܚܝܠ ܐܢܐ ܘܪܬܝܬ ܐܢܐ 21
Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”
ܐܢܬܘܢ ܕܝܢ ܐܬܩܪܒܬܘܢ ܠܛܘܪܐ ܕܨܗܝܘܢ ܘܠܡܕܝܢܬܐ ܕܐܠܗܐ ܚܝܐ ܠܐܘܪܫܠܡ ܕܒܫܡܝܐ ܘܠܟܢܫܐ ܕܪܒܘܬܐ ܕܡܠܐܟܐ 22
Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka.
ܘܠܥܕܬܐ ܕܒܘܟܪܐ ܕܡܬܟܬܒܝܢ ܒܫܡܝܐ ܘܠܐܠܗܐ ܕܝܢܐ ܕܟܠ ܘܠܪܘܚܬܐ ܕܟܐܢܐ ܕܐܬܓܡܪܘ 23
Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro.
ܘܠܝܫܘܥ ܡܨܥܝܐ ܕܕܝܬܩܐ ܚܕܬܐ ܘܠܪܤܤ ܕܡܗ ܕܡܡܠܠ ܛܒ ܡܢ ܗܘ ܕܗܒܝܠ 24
Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.
ܐܙܕܗܪܘ ܗܟܝܠ ܕܠܡܐ ܬܫܬܐܠܘܢ ܡܢ ܡܢ ܕܡܠܠ ܥܡܟܘܢ ܐܢ ܓܝܪ ܗܢܘܢ ܠܐ ܐܬܦܨܝܘ ܕܐܫܬܐܠܘ ܡܢ ܕܡܠܠ ܥܡܗܘܢ ܒܐܪܥܐ ܚܕ ܟܡܐ ܚܢܢ ܐܢ ܢܫܬܐܠ ܡܢ ܡܢ ܕܡܠܠ ܥܡܢ ܡܢ ܫܡܝܐ 25
Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba?
ܐܝܢܐ ܕܩܠܗ ܐܪܥܐ ܐܙܝܥ ܗܫܐ ܕܝܢ ܡܠܟ ܘܐܡܪ ܕܬܘܒ ܚܕܐ ܙܒܢ ܐܢܐ ܐܙܝܥ ܠܐ ܒܠܚܘܕ ܐܪܥܐ ܐܠܐ ܐܦ ܫܡܝܐ 26
Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.”
ܗܕܐ ܕܝܢ ܕܐܡܪ ܚܕܐ ܙܒܢ ܡܚܘܝܐ ܫܘܚܠܦܐ ܕܗܢܘܢ ܕܡܬܙܝܥܝܢ ܡܛܠ ܕܥܒܝܕܐ ܐܢܘܢ ܕܢܩܘܘܢ ܗܢܘܢ ܕܠܐ ܡܬܙܝܥܝܢ 27
Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.
ܡܛܠ ܗܟܝܠ ܕܩܒܠܢ ܡܠܟܘܬܐ ܕܠܐ ܡܬܙܝܥܐ ܢܐܚܘܕ ܛܝܒܘܬܐ ܕܒܗ ܢܫܡܫ ܘܢܫܦܪ ܠܐܠܗܐ ܒܬܚܡܨܬܐ ܘܒܕܚܠܬܐ 28
Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha.
ܐܠܗܢ ܓܝܪ ܢܘܪܐ ܗܘ ܐܟܠܬܐ 29
Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.

< ܥܒܪ̈ܝܐ 12 >