< Roma 7 >

1 Sana iyiru ba linuana [in din liru nin na nit ale na yiru uduka] bara uduka din dortu nin nit nan nya na yirin in lai me?
Kodi simukudziwa abale kuti Malamulo ali ndi ulamuliro pa munthu pokhapokha ngati ali ndi moyo? Ine ndikuyankhula kwa anthu amene akudziwa Malamulo.
2 Ame uwani ni luma a terin nin lesse nan nya nisilin niluma ywase ulesse nnku, abuntu nannya ni silin ni luma.
Mwachitsanzo, Malamulo amati mkazi wokwatiwa ndi womangidwa ndi lamulo kwa mwamuna wakeyo nthawi yonse pamene mwamuna wakeyo ali moyo. Koma ngati mwamuna wake amwalira, mkaziyo ndi womasulidwa ku lamulo la ukwati.
3 Bara nan, nan nya kubi ko na ulsse di nin lai asa anuzu asu iluma nin mong ima yichi ghe ukilak. Asa ulesse nku anuzu ni silin nilumea na du ikilaki asa su ilumama nin mong uni.
Koma ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina pamene mwamuna wake ali moyo, amatchedwa wachigololo. Koma ngati mwamuna wakeyo amwalira, mkaziyo amasuka ku lamulo ndipo si wachigololo, ngakhale kuti wakwatiwa ndi mwamuna wina.
4 Bara nanere nwa na nin i wa ti munu anan kul bar uduka nan nyan Kirst, bara ina dofuzonu ligowe nin nin nat, bara ame, naiwafiya ghe nan nya nan ku, bara bara nan macha nono fiu Kutelle.
Chimodzimodzi inunso, abale anga, munafa ku Malamulo kudzera mʼthupi la Khristu, kuti mukwatiwe ndi wina, ndi Iye amene anauka kwa akufa kuti tibalire Mulungu chipatso.
5 Kube na ti wadi nakidowo wanuzu kamang nan nya niti niti nidowo bite. In nuzum duka bara tinan nut tuno nono kul.
Pakuti pamene tinkalamulidwa ndi khalidwe lathu lauchimo, zilakolako zauchimo zimene Malamulo anaziwutsa zinkagwira ntchito mʼmatupi mwathu kotero kuti zinabala imfa.
6 Nene ina nutun nari nan nyan duk a tinani naku nan nyan in chn bite na ti wa kif, bara ti nan su kata kapese nan nya in fip Kutelle, na nan nya in chin ukuse ba.
Koma tsopano tamasulidwa ku Malamulowo pakuti tinafa ku zimene zinkatimanga, ndipo Mzimu Woyera akutithandiza kutumikira Mulungu mʼnjira yatsopano ndipo osati mʼnjira yakale yolembedwa.
7 Ani iyari tima belle nene? Ani uduk kulapiari litime? Na uwa so nanin b. Vat nin nan, na inwa na yinin kulapi ba, sasana uduka b. Na inwa yiru iyiru iyari kunaniyizi sasa na uduke na bellin b, “Naubasu kunaniyizi ba,”
Nanga ife tinene chiyani? Kodi Malamulo ndi oyipa? Ayi. Nʼkosatheka! Kunena zoona, popanda Malamulo, ine sindikanazindikira tchimo. Pakuti sindikanadziwa kuti kusirira ndi tchimo ngati Malamulo sakananena kuti, “Usasirire.”
8 Tutun kulapi nayiru kubi nan nya in duka unare na dak nin vat intok kulapi nan nya nin. Tutun andi na Uduka di ba kulapin nkul
Koma chifukwa cha Malamulo uchimo unapeza mwayi owutsa mʼkati mwanga khalidwe lililonse la kusirira. Pakuti pakanapanda Malamulo, uchimo ukanakhala wopanda mphamvu.
9 so uurum in wa yita nin bai sa Uduka ne uduka dak kulapi koni na kuru kurun fita iminaku
Nthawi ina ndinali ndi moyo popanda Malamulo. Koma nditayamba kudziwa Malamulo, pomwepo uchimo unayamba kuphuka,
10 Uduka na una din wori ubani ulai unin na da nin kul.
ndipo ine ndinafa. Ine ndinazindikira kuti Malamulo omwe ankayenera kubweretsa moyo anabweretsa imfa.
11 Kulapi na yiru kubi nan nyan Uduka kurusuzu, nkoni na molii kitenen uduke.
Pakuti uchimo unapeza mwayi chifukwa cha Malamulo ndipo kudzera mʼMalamulowo, unandinyenga ndi kundiyika mu imfa.
12 Nani ushara di lau a uduka lau imon ichine nin chau. So urum in wa yita nin lai sa uduka, nene na uduka na da, kulapi koni na kuru ku fita immini nak,
Choncho lamulo ndi loyera, lolungama ndi labwino.
13 Nni nene imon ichine isoyi ukulla? Na nani b. Nani kulapi, bara in durso kulapi ari sai nan nyan ni mon igegeme. uni na dai nin kul bara nan nya induka kulapi na na nnzu kamang.
Kodi chomwe ndi chabwino tsopano chinasanduka imfa kwa ine? Si choncho ayi! Koma kuti uchimo uzindikirike kuti ndi uchimo unabala imfa mwa ine kudzera mu chomwe chinali chabwino, kotero kuti kudzera mu lamulo uchimo ukhale oyipa kopitirira.
14 Bara tiyiru o Usharawe di nin fip kutelle, vat nanin in di na kidow. Ina lewi udu lichi nan nya, kulapi.
Ife tikudziwa kuti Malamulo ndi auzimu; koma ine ndine munthu wofowoka chabe, wogulitsidwa ngati kapolo ku uchimo.
15 Bara iwon ile na idin suzuna in yirub. Imon ile na indi nin sun su. Na in nare indun sue ba imon ile nain nari inare indin sue.
Ine sindizindikira zimene ndimachita. Pakuti zimene ndimafuna kuchita sindizichita koma zimene ndimadana nazo ndi zimene ndimazichita.
16 Bara nani andi in din su iwon ile na in dimin suwe b. Men yinni nin woru ushara chau.
Ndipo ngati ndimachita zimene sindimafuna kuzichita, ndiye kuti ndikuvomereza kuti lamulo ndi labwino.
17 Bara nani na mere din suzu ininb, kulape na kudi in nan nya nigher.
Monga mmene zililimu, si inenso mwini amene ndimazichita zimenezi, koma tchimo limene lili mʼkati mwanga.
18 Bara nanin men nan nya kidowo nigh, na imon ichine duku b, bara usuu ni mon ichine di nmi vat nani na in wasa su ba.
Ine ndikudziwa kuti mwa ine mulibe kanthu kabwino, ndiye kuti mʼthupi langa lauchimo. Pakuti ndimafuna kuchita zabwino, koma ndimalephera kuzichita.
19 Bara imon ichine ile na in dinin su in s, indin su b, nani imon inanzang ile na in di nin suwa ba inere in din su.
Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
20 Nene asan insuimon ile na indi nin su b, to nanere nane din in sue b, vat nane kulere na kudi nan nya nighe.
Tsopano ngati ine ndimachita zimene sindikuzifuna, si inenso amene ndimazichita, koma ndi tchimo limene lili mʼkati mwanga.
21 In se nan nya ime likara lichine in di nin sun in su imon ichin, vat nanin imon inanzanghari di in me.
Tsono ndapeza kuti lamuloli likugwira ntchito. Ngakhale ndimafuna kuchita zabwino, zoyipa zili nane pomwepo.
22 In di nin liburi libo nin shara Kutelle bara uni ule na adi nan nya ni.
Mtima wanga umakondwera ndi lamulo la Mulungu.
23 Mmini yene umon uka'idari ugan di niti niti kidowo nighe udi likum nin ukai'da upeseh nan nya kibinai nighe aminin yirai kuchin bara ukai'da kulapi ule udi niti niti nidowo nighe.
Koma mʼkati mwanga ndimaona lamulo lina likugwira ntchito kulimbana ndi zomwe mtima wanga umavomereza. Lamulo limenelo landisandutsa wamʼndende walamulo la uchimo lomwe likugwira ntchito mʼkati mwa ziwalo zanga.
24 Ki kimong nameng! Ghari ba tuchu menku nan nya kidawo nkul?
Kalanga ine! Adzandipulumutsa ndani ku thupi la imfali?
25 Liburi libo kiti Kutelle bara Kirsti Yisa Chikila bit. Bara nani meng litini ghe in lon li kot mmaa dortu Ushara Kutell, in lon li kot tutung indortu uka'ida kulapi nin kidowo.
Atamandike Mulungu, amene amandipulumutsa kudzera mwa Yesu Khristu Ambuye athu! Kotero tsono, ineyo ndi mtima wanga ndimatumikira lamulo la Mulungu, koma ndi thupi langa ndimatumikira lamulo la uchimo.

< Roma 7 >