< Roma 12 >

1 Nin nani, ndi kuchukulu kitimine linana bara gbardang nkune kune Kutellẹ, nan nidowo mine ugutunu mmii, imon seru kiti Kutellẹ, bara unnere unni natimine kiti Kutellẹ, nso katamine nan nya Nfip Kutellẹ.
Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
2 Yenjen iwa dofin lidu inyi ulelẹ, kpilan atimine iso apese nan nya nibinayi mine, inan yinnọ imonirika na idi ichine, inseru, nin chasarak nnufi Kutellẹ. (aiōn g165)
Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn g165)
3 In din bellu, bara ubollu Kutellẹ. na iwani, bara umon nan nya mine wayiru litime zikiki akata ligan lọ na ina cheghe ku: Na ikpilza ukpilzu uchine, nafo na Kutellẹ na fulọ kogha ku ligan chiu kibinayi in yinnu sa uyenu me.
Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
4 Nafo na niti niti di kidowo kirum, vat niti nitẹ ko kame dumun katamẹ,
Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
5 Nanere tidi gbardang kidowo kirume nan nya Kirsti, tidin gangang vat nin yitu arumẹ.
Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
6 Bara na kogha dimun da diume na ubollu Kutellẹ na nighe. Andi uda diue fe ubellu nnu Kutellẹ'ri, na usu dert nin ligang nimon na ina fuloghemun nan nya inyinnu sa uyenu.
Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
7 Andi uda diufe usu nsu nanit katawari, na asu. Andi uda diu fe udursuzu kitẹri, na a dursuzo.
Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
8 Andi uda diu fe unizu nanit likara kibinayari, niza ani: Andi uda diu unizuari, nizafi tapp: Andi uda diu fe uwunun nbunari, su seng. Andi uda diu fe ulanzu nkune kuneri, su nin nayi abho.
Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
9 Na ussu mine wanso unrusuzu liti ba. Nari imon inanzan; minọ ilele na ichau.
Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
10 Ubellẹ nsu linuana, chiun ussu natimine na nibinayi; nbellen ghantinu na kogha ni gwana me.
Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
11 Nbellen kayiri, iwasu ku gwala ba; nbellen nruhu, uyita mas mas; Nbellen Chikilari, su kata me.
Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
12 Nan nya nayi akone, su liburi liboọ; nbellen nfizu nayi, nonkon nibinayi; nbellen nlira, na iwachin ba.
Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
13 Dan timunu achara tibukatu na nan nsali kulapi, nan atimine anan sesu namara.
Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
14 Tan alẹ na idin nizu munu uniu nmari; tizan nmanri na ulaana.
Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
15 Sun ayi abho nin nale na idi nayi abho gilan nin nalẹ na idi kuchulu.
Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
16 Sun lisosin limang nan nanit vat. Iwaso anan kpilluzu nghantinu nati tibau mine ba, seren anan toltunu nati. Iwa yita jijin nan nya kpilluzu mine ba.
Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
17 Yenjen iwa tunu imon inanza nin nimon inanza. Sun imon ichine kiti nanit vat.
Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
18 Andi uba sonani, son ligan likara mine mang nan nanit vat.
Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
19 Yenjen iwa tunnu atiminemu, linuana, nan tinanayi Kutellẹ libau. Iyerte na woro ''uttunu unanighari; nba tunnu; ubellun inchikilari.''
Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
20 ''Asa unan salin nsufe din lanzu kukpon, naghe alii. Asa ayin kotoghe, naghe asonọ. Uwasu nani, uma pitiringhe achalang nlari litime.''
Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
21 Na iwasun tinanzang lii likara mine ba, lewu likara tinanzang nin gegeme.
Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

< Roma 12 >