< 1 Ukorintiyawa 9 >

1 Na meng in shutu ba? Na Meng gono katawari ba? Na Meng wa yene Yisa Cikilari bite ba? Na anug hère katuwa nacara nighere nan nya Ncikilari ba?
Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi sindinamuone Ambuye athu Yesu? Kodi inu sindiye zotsatira za ntchito yanga mwa Ambuye?
2 Andi na Meng gono kadurari kiti namon ba, ai kiti mine ndi, bara anughere ba dursu annit meng gono kadura, nan nya Ncikilari.
Ngakhale kwa ena sindingakhale mtumwi, mosakayika ndine mtumwi kwa inu! Poti inu ndi chizindikiro cha utumwi wanga mwa Ambuye.
3 Ulelere ukesu kiti nale nge na udi dumu zuni.
Kwa iwo wofuna kundizenga milandu ndimawayankha kuti:
4 Na arike nwanya tileoti sono ba?
Kodi ife tilibe ulamuliro wakudya ndi kumwa?
5 Na wanya yira awani ba anan nyinnu Kutellẹ nafo kagisin nanan kadura, nin nuwana nan nya Ncikilari ame Bitrus.
Kodi ife tilibe ulamuliro wotenga mkazi wokhulupirira nʼkumayenda naye monga amachitira atumwi ena ndi abale awo a Ambuye ndiponso Kefa?
6 Sa Barnabas nin mi arikere ba su katuwa casa?
Kodi kapena ine ndekha ndi Barnaba ndiye tikuyenera kugwira ntchito kuti tipeze zotisowa?
7 Ghari di katuwa nafo kusoja, ame leo nin litime? Ghari ba bilisu imon nan nya a wanya aleo ba? Sa Ghari basu libiya ninab sa uwuru asonu madare?
Ndani angagwire ntchito ya usilikali namadzipezera yekha zofunika zonse? Kodi ndani amadzala mpesa koma wosadyako zipatso zake? Ndani amaweta nkhosa koma wosamwako mkaka wake?
8 Ndi belle ule imone bara likara nnit usurne? Na uduka bellin nano ba?
Kodi moti zimene ndikunenazi ndimaganizo a umunthu chabe? Kodi Malamulo sakunena chimodzimodzinso?
9 Nafo na udi ninyerte nduka Musa, “Yenje uwa tursu fina unu kubi na adi katuwa kunen nileo.” Kidege innari cas Kutellẹ min nania?
Popeza analemba mʼMalamulo a Mose kuti, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.” Kodi pamene Mulungu ananena zimenezi ankalabadira za ngʼombe zokha?
10 Na ame din nliru kitene bite ba? Iwa nyertin bara arikere, bara ulle na adi nikawa na asu nin ti kibinai, unan su kinorso na asu nin ti kibinai nworu aba se kubi ngirbe.
Ndithu Iyeyo amanena za ifenso, kodi si choncho? Inde, izi anazilemba chifukwa cha ife, pakuti wolima ndiponso wopuntha, onsewo amagwira ntchito mwachiyembekezo chodzagawana zokololazo.
11 Asa ti bilisa imon Ruhu nanya mine, uba yitu gbardang kagha arike nwase imon lisosin nye kiti mine?
Ngati tidzala mbewu yauzimu pakati panu, kodi ndi chovuta kwambiri kuti tikolole zosowa zathu kuchokera kwa inu?
12 Andi amon di pirizu imon na idi imine kiti mine, na arike dumun nile na ikatin ba? Na nanere ba, na tina se ileli imone ba. Tima teru ayi bara ti wa wantin uliru nlai Kristi.
Ngati ena ali ndi ufulu wothandizidwa ndi inu, kodi ife sitikuyenera kukhala nawo ufulu ochulukirapo? Koma ife sitinagwiritse ntchito ufulu umenewu. Mʼmalo mwake timangodzichitira chilichonse posafuna kutsekereza ena kumva Uthenga Wabwino wa Khristu.
13 Na anug yiru ba nworu allenge na idin su katuwa kutyin nlira iba se imonli mine kutyin nlire? Inung alle na idi katuwa kitene nbadagi, adi nli imonli me kikene bagade?
Kodi simukudziwa kuti wogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amapeza chakudya chawo mʼNyumbamo, ndipo kuti otumikira pa guwa lansembe amagawana zimene zaperekedwa pa guwa lansembelo.
14 Nanere, Kutellẹ wa ni uduka aworo ulle na adin bellu nlai, iba se imonli me kiti nbellu nliru nlai.
Chomwechonso Ambuye akulamula kuti wolalikira Uthenga Wabwino azilandira thandizo lawo polalikira Uthenga Wabwinowo.
15 Vat nin nani, nan nsa se imomon nanya nile imone vatt ile imone bara inan su menku imomon ba, ukatin nku nin nworo anung yene ufo figiri nighe so uhem.
Koma ine sindinagwiritse ntchito ufulu woterewu. Sindikulemba izi ndi chiyembekezo choti mundichitire zoterezi. Kuli bwino ndife kusiyana nʼkuti wina alande zomwe ndimazinyadira.
16 Asa ndin bellu uliru nlai, na nile imon na iba fo figiri ba, bara ikifoi nsu nani, kash nin mi asa na nbelle uliru a nlai ba.
Komatu ndikamalalikira Uthenga Wabwino, sindingadzitamandire popeza ndimawumirizidwa kulalikira. Tsoka kwa ine ngati sindilalikira Uthenga Wabwino!
17 Bare nwa su illenge imone nani nin kibinai kirum, mba seru ulada andi na nin kibinai kirum ba ndu nin katuwa kanga na iwa nie.
Ngati ndikugwira ntchitoyi mwakufuna kwanga, ndili ndi mphotho; koma ngati si mwakufuna kwanga, ndiye kuti ntchitoyi ndi Ambuye anandipatsa.
18 Iyaghari ulada nighe? nworu uwa bellu uliru nlai meng ba ni uliru nlai sa useru nimomon, nan baseru ile imon na nyene inaghari nanya nliru kulelle.
Tsono mphotho yanga ndi chiyani? Ndi iyi: kuti polalikira Uthenga Wabwino ndiwupereke kwaulere komanso kuti ndisagwiritse ntchito ufulu wanga polalikira uthengawo.
19 Bara nani meng shutu na cara na nit vat, nlawa kucin kiti nanit vat, bara nnan wunno annit vat.
Ngakhale ndine mfulu ndipo sindine kapolo wa munthu, ndimadzisandutsa kapolo wa aliyense kuti ndikope ambiri mmene ndingathere.
20 Kiti na yahudawa so nafo kuyahudawa, bara nna wuno ayahudawa, kiti na ilenge na imin nduka, nso nafoo allenge na imin (vat nin nani, na meng min ushara ba) nnan wunun alle na imnin ushara.
Kwa Ayuda ndimakhala ngati Myuda kuti ndikope Ayuda. Kwa olamulidwa ndi Malamulo ndimakhala ngati wolamulidwa nawo (ngakhale kuti sindine wolamulidwa ndi Malamulowo) kuti ndikope amene amalamulidwa ndi Malamulo.
21 Kiti nale na isali nin nshara, meng wan so nafo unan nsalin nshara. (na Meng litinighe na nta unan nsalin nshara ba kiti Kutellẹ ndi nanya nduka Kristi) nnan wunno alle na isali nan nya nshara.
Kwa amene alibe Malamulo ndimakhala wopanda Malamulo (ngakhale kuti sindine wopanda Malamulo a Mulungu koma ndili pansi pa ulamuliro wa Khristu) kuti ndikope wopanda Malamulo.
22 Kiti nan nsali likara, meng so unan sali likara anan sali likara nso imon vat kiti anit vat bara ko niyagh Meng tucu among.
Kwa ofowoka ndimakhala wofowoka, kuti ndikope ofowoka. Ndimachita zinthu zilizonse kwa anthu onse kuti mwanjira ina iliyonse ndipulumutse ena.
23 Nchin su imon vat bbara ubellen nliru Kutellẹ, bara Meng ma nan se upiru nan nya imari me.
Ndimachita zonsezi chifukwa cha Uthenga Wabwino, kuti ndigawane nawo madalitso ake.
24 Na anung yiru nwo nanyan cum vat anang cume din su ucume, ama waseme minere asa asere uduke? Bara nani sun ucum ilii uduke.
Kodi simukudziwa kuti pa mpikisano wa liwiro onse amathamanga ndithu, koma mmodzi yekha ndiye amalandira mphotho? Motero thamangani kuti mupate mphotho.
25 Unan katwa ncum din zulu kidowo me ayita nin minu nnu nanyan vat nzulu kidowo me. Inung dinsu iseru uduk ulenge na udin nanuzu, ama arik din cum tinan seru uduk un salin nanuzu.
Aliyense wochita mpikisano amakonzekera mwamphamvu. Amachita izi kuti alandire mphotho yankhata yamaluwa yomwe imafota. Koma ife timachita izi kuti tilandire mphotho yosafota.
26 Bara nani, na meng din cum sa ukpiluzu ba a na ndas libau nfunu ba.
Choncho sindithamanga monga wothamanga wopanda cholinga; komanso sindichita mpikisano wankhonya monga munthu amene amangomenya mophonya.
27 Ama meng kifu kidowo ning nning ta kinin kucin, bara kimalin wazi ninghe kiti namong, na meng wang iwa nazue mung ba.
Ine ndimazunza thupi langa ndi kulisandutsa kapolo kuti nditatha kulalikira ena, ineyo ndingadzapezeke wosayenera kulandira nawo mphotho.

< 1 Ukorintiyawa 9 >